20 ndipo wansembe aziweyula nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ici ncopatulikira wansembe, pamodzi ndi nganga ya nsembe yoweyula, pamodzi ndi mwendo wa nsembe yokweza; ndipo atatero Mnaziri amwe vinyo.
21 Ici ndi cilamulo ca Mnaziri wakuwinda, ndi ca copereka cace ca Yehova cifukwa ca kusala kwace, pamodzi naco cimene dzanja lace likacipeza; azicita monga mwa cowinda cace anaciwinda, mwa cilamulo ca kusala.
22 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
23 Nena ndi Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Uzidalitsa ana a Israyeli motero; uziti nao,
24 Yehova akudalitse iwe, nakusunge;
25 Yehova awalitse nkhope yace pa iwe, nakucitire cisomo;
26 Yehova akweze nkhope yace pa iwe, nakupatse mtendere.