10 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Angakhale munthu wa inu kapena wa mibadwo yanu, adetsedwa, cifukwa ca mtembo, kapena pokhala paulendo, koma azicitira Yehova Paskha.
11 Mwezi waciwiri, tsiku lace lakhumi ndi cinai, madzulo, aucite; audye ndi mkate wopanda cotupitsa ndi msuzi wowawa.
12 Asasiyeko kufikira m'mawa, kapena kuthyolapo pfupa; aucite monga mwa lemba lonse la Paskha.
13 Munthu akakhala woyera, wosakhala paulendo, koma akaleka kucita Paskha, amsadze munthuyo kwa anthu a mtundu wace; popeza sanabwera naco copereka ca Yehova pa nyengo yace yoikidwa, munthuyu asenze kucimwa kwace.
14 Ndipo mlendo akakhala mwa inu, nakacitira Yehova Paskha, azicita monga mwa lemba la Paskha, ndi monga mwa ciweruzo cace; lemba likhale limodzi kwa inu, ndi kwa mlendo, ndi kwa wobadwa m'dziko.
15 Ndipo tsiku loutsa kacisi mtambo unaphimba kacisi, ndiwo cihema cokomanako; ndipo madzulo padaoneka pakacisi ngati moto, kufikira m'mawa.
16 Kudatero kosalekeza; mtambo umaciphimba, ndimoto umaoneka usiku,