1 PACIYAMBI Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 Dziko lapansi ndipo linali lopanda kanthu; ndipo mdima unali pamwamba pa nyanja; ndipo mzimu wa Mulungu unaliokufungatira pamwamba pa madzi.
3 Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.
4 Ndipo anaona Mulungu kuti kuyerako kunali kwabino: ndipo Mulungu analekanitsa kuyera ndi mdima.