Genesis 49 BL92

Yakobo adalitsa ana ace namwalira

1 Ndipo Yakobo anaitana ana ace amuna, nati, Sonkhanani inu, kuti ndikuuzeni inu cimene cidzakugwerani inu masiku akudzawo.

2 Sonkhanani, tamvani, ana amuna a Yakobo:Tamverani Israyeli atate wanu:

3 Rubeni, ndiwe woyamba wanga, mphamvu yanga ndi ciyambi ca mphamvu yanga;Ulemu wopambana, ndi mphamvu yopambana.

4 Wobwabwada ngati madzi; sudzapambana;Cifukwa unakwera pa kama wa atate wako;Pamenepo unaipitsapo; anakwera paja ndigonapo.

5 Simeoni ndi Levi ndiwo abale;Zida za mphulupulu ndizo malupanga ao.

6 Mtima wangawe, usalowe mu ciungwe cao;Ulemerero wanga, usadziphatike pa masonkhano ao;Cifukwa m'kukwiya kwao anapha munthu,M'kufuna kwao anapundula ng'ombe.

7 Kutembereredwekukwiyakwao, cifukwa kunali koopsya;Ndi kupsya mtima kwao, cifukwa kunali kwankharwe;Ndidzawagawanitsa m'YakoboNdidzabalalitsa iwo m'Israyeli.

8 Yuda, abale ako adzakuyamika iwe;Dzanja lako lidzakhala pa khosi la adani ako;Ana amuna a atate wako adzakuweramira.

9 Yuda ndi mwana wa mkango,Kucokera kuzomotola, mwananga, wakwera;Anawerama pansi, anabwatama ngati mkango,Ndipo ngati mkango waukazi; ndani adzamukitsa iye?

10 Ndodo yacifumu siidzacoka mwa Yuda,Kapena wolamulira pakati pa mapazi ace,Kufikira atadza Silo;Ndipo anthu adzamvera iye.

11 Adamanga mwana wa kavalo wace pampesa,Ndi mwana wa buru wace pa mpesa wosankhika;Natsuka malaya ace m'vinyo,Ndi copfunda cace m'mwazi wa mphesa.

12 Maso ace adzafiira ndi vinyo,Ndipo mana ace adzayera ndi mkaka.

13 Zebuloni adzakhala m'doko la kunyanja;Ndipo iye adzakhala doko la ngalawa;Ndipo malire ace adakhala pa Zidoni.

14 Isakara ndiye buru wolimba,Alinkugona pakati pa makola;

15 Ndipo anaona popumulapo kuti panali pabwino,Ndi dziko kuti linali lokondweretsa;Ndipo anaweramitsa phewa lace kuti anyamule,Nakhala kapolo wakugwira nchito ya msonkho,

16 Dani adzaweruza anthu ace,Monga limodzi la mafuko a Israyeli.

17 Dani adzakhala njoka m'khwalala,Songo panjira,Imene iluma zitende za kavalo,Kuti womkwera wace agwe cambuyo.

18 Ndadikira cipulumutso canu, Yehova.

19 Ndi Gadi, acifwamba adzampsinja iye;Koma iye adzapsinja pa citende cao.

20 Ndi Aseri, cakudya cace ndico mafuta,Ndipo adzapereka zolongosoka zacifumu.

21 Nafitali ndi nswala yomasuka;Apatsa mau abwino.

22 Yosefe ndi nthambi yobala,Nthambi yobala pambali pa kasupe;Nthambi zace ziyangayanga palinga.

23 Eni uta anabvutitsa iye kwambiri,Namponyera iye, namzunza:

24 Koma uta wace unakhala wamphamvu,Ndi mikono ya manja ace inalimbitsidwaNdi manja a Wamphamvu wa Yakobo.(Kucokera kumeneko ndi mbusa, mwala wa Israyeli,)

25 Ndi Mulungu wa atate wako amene adzakuthangata iwe,Ndi Wamphamvuyonse, amene adzakudalitsa iweNdi madalitso a Kumwamba,Madalitso a madzi akuya akukhala pansi,Madalitso a mabere, ndi a mimba.

26 Madalitso a atate wakoApambana mphamvu ndi madalitso a makolo anga,Kufikira ku malekezero a patari a mapiri a cikhalire;Adzakhala pa mutu wa Yosefe,Ndi pakati pa mutu wa iye amene ali wolekanitsidwa ndi abale ace.

27 Benjamini ndiye mmbulu wakulusalusa;M'mamawa adzadya comotola,Madzulo adzagawa zofunkha.

28 Awa onse ndiwo mafuko khumi ndi awiri a Israyeli: izo ndizo zomwe ananena kwa iwo atate wao nawadalitsa; yense monga mdalitso wace anawadalitsa.

29 Ndipo analangiza iwo nati kwa iwo, Ine nditi ndisonkhanizidwe kwa anthu a mtundu wanga; mundiike ine pamodzi ndi makolo anga m'phanga liri m'munda wa Efroni Mhiti,

30 m'phanga liri m'munda wa Makipela, umene uli patsogolo pa Mamre, m'dziko la Kanani, limene Abrahamu analigula kwa Efroni Mhiti pamodzi ndi munda, likhale poikira pace:

31 pamenepo anaika Abrahamu ndi Sara mkazi wace; pamenepo anaika Isake ndi Rebeka mkazi wace: pamenepo ndinaika Leya:

32 munda ndi phanga liri m'menemo, zinagulidwa kwa ana a Heti.

33 Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ace amuna, anafunya mapazi ace pakama, natsirizika, nasonkhanizidwa kwa anthu a mtundu wace.