8 Ndipo Yehova anabalalitsa iwo pa dziko lonse lapansi, ndipo analeka kumanga mudzi.
9 Cifukwa cace anacha dzina lace Babele; pakuti kumeneko Yehova anasokoneza cinenedwe ca dziko lonse lapansi; kuyambira pamenepo Yehova anabalalitsa iwo pa dziko lonse lapansi.
10 Mibadwo ya Semu ndi iyi: Semu anali wa zaka zana limodzi ndipo anabala Aripakasadi, citapita cigumula zaka ziwiri;
11 ndipo Semu anakhala ndi moyo zaka mazana asanu, atabala Aripakasadi, nabala ana amuna ndi akazi.
12 Ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zisanu, nabala Sela;
13 ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Sela, nabala ana amuna ndi akazi.
14 Ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala Ebere;