3 Ndipo Yehova anati kwa Yakobo, Bwera ku dziko la atate wako, ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakhala ndi iwe.
4 Ndipo Yakobo anatumiza naitana Rakele ndi Leya adze kubusa ku zoweta zace,
5 ndipo anati kwa iwo, Ndiona ine nkhope ya atate wanu kuti siindionekera ine monga kale; koma Mulungu wa atate wanga anali ndi ine.
6 Ndipo inu mudziwa kuti ndi mphamvu zanga zonse ndatumikira atate wanu.
7 Ndipo atate wanu wandinyenga ine, nasinthanitsa malipilo anga kakhumi; koma Mulungu sanamlole iye andicitire ine coipa.
8 Akati cotero, Zamathotho-mathotho zidzakhala malipilo ako, zoweta zonse zinabala zamathotho-mathotho; ndipo akati iye cotere, Zamipyololo-mipyololo zidzakhala malipilo ako, ziweto zonse zinabala mipyololo-mipyololo.
9 Comweco Mulungu anazicotsa zoweta za atate wanu, nandipatsa ine.