15 Ndipo anacha dzina lace la pamalo pamene Mulungu ananena ndi iye, Beteli.
16 Ndipo anacokera ku Beteli: ndipo panatsala nthawi asanafike ku Efrati: ndipo Rakele anabala nabvutidwa.
17 Ndipo panali pamene anabvutidwa, namwino anati kwa iye, Usaope: pakuti udzakhala ndi mwana wina wamwamuna.
18 Ndipo pakutsirizika iye, pakuti anamwalira, anamucha dzina lace Benoni; koma atate wace anamucha Benjamini.
19 Ndipo anafa Rakele, naikidwa pa njira va ku Efrati (ndipo Betelehemu),
20 Ndipo Yakobo anaimiritsa mwala pamanda pace: umenewo ndi coimiritsa ca pa manda a Rakele kufikira lero.
21 Ndipo Israyeli anapita namanga hema wace patseri pa nsanja ya Edere.