22 Ndipo panali pamene Israyeli anakhala m'dzikomo, Rubeni anamuka nagona ndi Biliha, mkazi wamng'ono wa atate wace: ndipo Israyeli anamva.Ana amuna a Yakobo anali khumi ndi awiri:
23 ana amuna a Leya: ndiwo Rubeni mwana woyamba wa Yakobo, ndi Simeoni ndi Levi, ndi Yuda, ndi Zebuloni, ndi Isakara;
24 ana amuna a Rakele: ndiwo Yosefe ndi Benjamini;
25 ana amuna a Biliha mdzakazi wace wa Rakele: ndiwo Dani ndi Nafitali;
26 ndipo ana amuna a Zilipa mdzakazi wace wa Leya: ndiwo Gadi ndi Aseri: amenewo ndi ana amuna a Yakobo amene anabala iye m'Padanaramu.
27 Ndipo Yakobo anafika kwa Isake atate wace ku Mamre, ku KiriyatiAriba (ndiwo Hebroni) kumene anakhala Abrahamu ndi Isake.
28 Ndipo masiku a Isake anali zaka zana limodzi kudza makumi asanu ndi atatu.