1 Mibadwo ya Esau (ndiye Edomu) ndi iyi:
2 Esau anatenga akazi ace a ana akazi a m'Kanani: Ada mwana wamkazi wa Eloni Mhiti, ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mwana wamkazi wa Zibeoni Mhivi;
3 ndi Basemati mwana wamkazi wa lsmayeli, mlongo wace wa Nabayoti.
4 Ndipo Ada anambalira Esau Elifazi; ndipo Basemati anabala Reueli;