19 Ndipo anati wina ndi mnzace, Taonani, alinkudza mwini maloto uja.
20 Tiyeni tsopano timuphe iye timponye m'dzenje, ndipo tidzati, Wajiwa ndi cirombo; ndipo tidzaona momwe adzacita maloto ace.
21 Ndipo Rubeni anamva nampulumutsa iye m'manja mwao; nati, Tisamuphe iye,
22 Ndipo Rubeni anati kwa iwo, Musakhetse mwazi; mponyeni iye m'dzenjemo m'cipululu muno, koma musamsamulire iye manja: kuti ampulumutse iye ra'manja mwao, ambwezenso kwa atate wace.
23 Ndipo panali pamene Yosefe anafika kwa abale ace, anambvula Yosefe malaya ace, malaya amwinjiro amene anabvala iye;
24 ndipo anamtenga iye, namponya m'dzenjemo; m'dzenjemo munalibe kanthu, munalibe madzi m'menemo.
25 Ndipo iwo anakhala pansi kuti adye cakudya; ndipo anatukula maso ao, nayang'ana, ndipo taonani, ulendo wa Aismayeli anacokera ku Gileadi ndi ngamila zao, zilinkunyamula zonunkhira ndi mafuta amankhwala ndi libano alinkumuka kutsikira nazo ku Aigupto.