1 Ndipo panali nthawi yomweyo, kuti Yuda anatsikira kwa abale ace nalowa kwa M-adulami, dzina lace Hira.
2 Ndipo Yuda anaona kumeneko mwana wamkazi wa Mkanani dzina lace Sua: ndipo anamtenga, nalowa kwa iye.
3 Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Eri.
4 Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Onani.
5 Ndipo anabalanso mwana wamwamuna, namucha dzina lace Sela: ndipo iye anali pa Kezibi pamene mkazi anambala iye,
6 Ndipo Yuda anamtengera Eri mwana wace woyamba mkazi, ndipo dzina lace ndilo Tamara.
7 Koma Eri mwana wace woyamba wa Yuda anali woipa pamaso pa Yehova: ndipo Yehova anamupha iye.