3 Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Eri.
4 Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Onani.
5 Ndipo anabalanso mwana wamwamuna, namucha dzina lace Sela: ndipo iye anali pa Kezibi pamene mkazi anambala iye,
6 Ndipo Yuda anamtengera Eri mwana wace woyamba mkazi, ndipo dzina lace ndilo Tamara.
7 Koma Eri mwana wace woyamba wa Yuda anali woipa pamaso pa Yehova: ndipo Yehova anamupha iye.
8 Ndipo Yuda anati kwa Onani, Lowani naye mkazi wa mbale wako, ndi kumcitira mkazi zoyenera mphwace wa mwamuna wace, ndi kumuukitsira mkuru wako mbeu.
9 Ndipo Onani anadziwa kuti mbeu siidzakhala yace: ndipo panali pamene iye analowana naye mkazi wa mbale wace, kuti anaitaya pansi, kuti angampatse mbeu kwa mkuru wace.