4 Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Onani.
5 Ndipo anabalanso mwana wamwamuna, namucha dzina lace Sela: ndipo iye anali pa Kezibi pamene mkazi anambala iye,
6 Ndipo Yuda anamtengera Eri mwana wace woyamba mkazi, ndipo dzina lace ndilo Tamara.
7 Koma Eri mwana wace woyamba wa Yuda anali woipa pamaso pa Yehova: ndipo Yehova anamupha iye.
8 Ndipo Yuda anati kwa Onani, Lowani naye mkazi wa mbale wako, ndi kumcitira mkazi zoyenera mphwace wa mwamuna wace, ndi kumuukitsira mkuru wako mbeu.
9 Ndipo Onani anadziwa kuti mbeu siidzakhala yace: ndipo panali pamene iye analowana naye mkazi wa mbale wace, kuti anaitaya pansi, kuti angampatse mbeu kwa mkuru wace.
10 Koma cimene iye anacita cinali coipa pamaso pa Mulungu, ndipo anamupha iyenso.