1 Ndipo panali zitapita izi, wopereka cikho wa mfumu ya Aigupto ndi wophika mkate wace anamcimwira mbuye wao mfumu ya Aigupto.
2 Ndipo Farao anakwiyira akuru ace awiriwo wamkuru wa opereka cikho, ndi wamkuru wa ophika mkate.
3 Ndipo anaika iwo asungidwe m'nyumba ya kazembe wa alonda, m'kaidi, umo anamangidwa Yosefe.
4 Ndipo kazembe wa alonda anapereka iwo kwa Yosefe, ndipo iye anawatumikira iwo: ndipo anakhala nthawi mosungidwamo.
5 Ndipo analota maloto onse awiri, yense lata lace, usiku umodzi, yense monga mwa kumasulira kwa loto lace, wopereka cikho ndi wophika mkate wa mfumu ya Aigupto, amene anamangidwa m'kaidi.
6 Ndipo Yosefe analowa kwa iwo m'mawa, nawaona iwo, taonani, anali oziya.
7 Ndipo anafunsa akuru a Farao osungidwa naye m'nyumba ya mbuyace, kuti, Nkhope zanu zagwa bwanji lero?