9 Ndipo wopereka cikho wamkuru anafotokozera Yosefe loto lace, nati kwa iye, M'kulota kwanga, taona, mpesa unali pamaso panga:
10 ndipo m'mpesamo munali nthambi zitatu: ndipo unali wonga unaphuka, ndipo maluwa ace anaphuka; nabala matsamvu ace mphesa zakuca:
11 ndipo cikho ca Farao cinali m'dzanjalanga: ndipo ndinatenga mphesa, ndi kufinyira m'cikho ca Farao ndi kupereka cikho m'dzanja la Farao.
12 Ndipo Yosefe anati kwa iye, Mmasuliro wace ndi uwu: nthambi zitatu ndizo masiku atatu;
13 akali masiku atatu Farao adzatukula mutu wako, nadzabwezera iwe nchito yako; ndipo udzapereka cikho ca Farao m'dzanja lace, monga kale lomwe m'mene unali wopereka cikho cace.
14 Koma undikumbukire ine m'mene kudzakhala bwino ndi iwe, ndipoundicitiretu ine kukoma mtima: nundichule ine kwa Farao, nunditurutse ine m'nyumbamu:
15 cifukwa kuti ndinabedwa ndithu m'dziko la Ahebri; ndiponso pano sindinacite kanthu kakundiikira ine m'dzeniemu.