30 Ndipo Yosefe anafulumira, cifukwa mtima wace unakhumbitsa mphwace, ndipo mafuna polirira; nalowa m'cipinda ace naliramo.
31 Ndipo anasamba ikhope yace, naturuka; ndipo anadziletsa, nati, Ikani cakudya.
32 Ndipo anamuikira iye cace pa yekha, ndi wo cao pa okha, ndi Aaigupto ikudya naye cao pa okha; cifukwa aigupto sanathei kudya cakudya pamodzi ndi Ahebri: cifukwa kucita comweco nkunyansira Aaigupto.
33 Ndipo anakhala pamaso pace, woyanba monga ukuru wace, ndi wanng'ono mensa ung'ono wace; ndipo mazizwa wina ndi wina.
34 Ndipo mawagawira mitanda ya patsogolo pace; koma mtanda wa Benjamini maposa mitanda ya onsewo kasanu. Ndipo anamwa, nasekera pamodzi ndi iye.