4 Masiku ace Adamu atabala Seti, anali zaka mazana asanu ndi atatu; ndipo anabala ana amuna ndi akazi.
5 Masiku ace onse anakhala ndi moyo Adamu anali zaka mazana asanu ndi anai, kudza makumi atatu; ndipo anamwalira.
6 Ndipo Seti anakhala ndi moyo zaka zana kudza zisanu, nabala Enosi;
7 ndipo Seti anakhala ndi moyo, atabala Enosi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza zisanu ndi ziwiri: ndipo anabala ana amuna ndi akazi:
8 masiku ace onse a Seti anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi ndi ziwiri; ndipo anamwalira.
9 Ndipo Enosi anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi anai, nabala Kenani;
10 ndipo anakhala ndi moyo Enosi, atabala Kenani, zaka mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi zisanu: ndipo anabala ana amuna ndi akazi.