14 Ndipo ataika atate wace, Yosefe mabwera ku Aigupto, iye ndi abale ace, ndi onse amene anakwera pamodzi naye kukaika atate wace.
15 Ndipo pamene abale ace a Yosefe anaona kuti atate wao anafa, anati, Kapena Yosefe adzatida ife, ndipo adzatibwezera ife zoipa zonse tidamcitira iye.
16 Ndipo anatumiza mthenga kwa Yosefe kuti, Atate wathu asanafe analamulira, kuti,
17 Muziti cotero kwa Yosefe, Mukhululukiretu tsopano kulakwa kwa abale anu, ndi kucimwa kwao, cifukwa kuti anakucitirani inu coipa; tsopano mutikhululukiretu kulakwa kwa aka polo a Mulungu wa atate wanu. Ndipo Yosefe analira pamene iwo ananena ndi iye.
18 Ndiponso abale ace anamuka namgwadira pamaso pace; nati, Taonani, ife ndife akapolo anu.
19 Ndipo Yosefe anati kwa iwo, Musaope; pakuti ndiri ine kodi m'malo a Mulungu?
20 Koma inu, munandipangira ine coipa; koma Mulungu anacipangira cabwino, kuti kucitike monga lero, kupulumutsa amoyo anthu ambiri,