15 ndipo ndidzakumbukira pangano langa limene liri ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo; ndipo madzi sadzakhalanso konse cigumula cakuononga zamoyo zonse.
16 Ndipo utawo udzakhala m'mtambo; ndipo ndidzauyang'anira kuti ndikumbukire pangano lacikhalire liri ndi Mulungu ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo pa dziko lapansi.
17 Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Ici ndici cizindikiro ca pangano ndalikhazikitsa popaogana ndi Ine ndi zamoyo zonse za pa dziko lapansi.
18 Ndi ana amuna a Nowa amene anaturuka m'cingalawa ndiwo Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti: Hamu ndiye atate wace wa Kanani.
19 Amenewa ndiwo ana amuna atatu a Nowa: ndiwo anafalikira dziko lonse lapansi.
20 Ndipo anayamba Nowa kukhala munthu wakulima nthaka, ndipo analima munda wamphesa:
21 namwa vinyo wace, naledzera; ndipo anali wamarisece m'kati mwa bema wace.