32 Ndipo pokhala ana a Israyeli m'cipululu, anapeza munthu wakufuna nkhuni tsiku la Sabata.
33 Ndipo amene adampezawo alinkufuna nkhuni anabwera naye kwa Mose ndi Aroni, ndi kwa khamu lonse.
34 Ndipo anathanga wamsunga, popeza sicinanenedwa coyenera kumcitira iye.
35 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Amuphe munthuyu ndithu; khamu lonse limponye miyala kunja kwa cigono.
36 Pamenepo khamu lonse linamturutsa kunja kwa cigono, ndi kumponya miyala, ndipo anafa; monga Yehova adauza Mose.
37 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
38 Nena ndi ana a Israyeli, nuwauze kuti adziombere mphonje m'mphepete mwa zobvala zao, mwa mibadwo yao, naike pamphonje m'mphepetemo thonje lamadzi.