45 Ana a Beriya ndiwo: Heberi, ndiye kholo la banja la Aheberi; Malikiyeli, ndiye kholo la banja la Amalikiyeli.
46 Ndipo dzina la mwana wamkazi wa Aseri ndiye Sera.
47 Iwo ndiwo mabanja a ana amuna a Aseri monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.
48 Ana amuna a Nafitali monga mwa mabanja ao ndiwo: Yazeli, ndiye kholo la banja la Ayazeli; Guni, ndiye kholo la banja la Aguni;
49 Yezeri, ndiye kholo la banja la Ayezeri; Silemu, ndiye kholo la banja la Asilemu.
50 Iwo ndiwo mabanja a Nafitali, monga mwa mabanja ao; ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana anai.
51 Iwo ndiwo owerengedwa ao a ana a Israyeli, zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu cimodzi kudza mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu.