54 Ocurukawo, uwacurukitsire colowa cao; ocepawo uwacepetsere colowa cao; ampatse yense colowa cace monga mwa owerengedwa ace.
55 Koma aligawe ndi kucita maere; colowa cao cikhale monga mwa maina a mafuko a makolo ao,
56 Agawire ocuruka ndi ocepa colowa cao monga mwa kucita maere.
57 Ndipo awa ndi owerengedwa ao a Alevi monga mwa mabanja ao: Gerisoni, ndiye kholo la banja la Agerisoni; Kohati, ndiye kholo la banja la Akohati; Merari, ndiye kholo la banja la Amerari.
58 Awa ndi mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, banja la Akohati. Ndipo Kohati anabala Amiramu.
59 Ndipo dzina lace la mkazi wace wa Amiramu ndiye Yokebedi, mwana wamkazi wa Levi, wobadwira Levi m'Aigupto; ndipo iye anambalira Amiramu Aroni ndi Mose, ndi Miriamu mlongo wao.
60 Ndipo Nadabu ndi Abihu, Eleazara ndi ltamara anabadwira Aroni.