43 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu kuti agwire nchito m'cihema cokomanako,
44 owerengedwa ao monga mwa mabanja ao, ndiwo zikwi zitatu ndi mazana awiri.
45 Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.
46 Owerengedwa onse a Alevi, amene Mose ndi Aroni ndi akalonga a Israyeli anawawerengera, monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,
47 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa kugwira nchito ya utumikiwu, ndiyo nchito ya akatundu m'cihema cokomanako;
48 owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu mphambu makumi asanu ndi atatu.
49 Anawawerenga monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose, onse monga mwa nchito zao, ndi monga mwa akatundu ao; anawawerenga monga momwe Yehova adauza Mose.