1 Mau a Yehova anandidzeranso, ndi kuti,
2 Wobadwa ndi munthu iwe, ukhala pakati pa nyumba yampanduko, yokhala nao maso akuonera, koma osaona; ndi makutu akumvera, koma osamva; pakuti iwo ndiwo nyumba yampanduko.
3 Potero wobadwa ndi munthu iwe, udzikonzeretu akatundu a pa ulendo wa kundende, nucoke usana pamaso pao, ucoke pakhala iwepo kumka malo ena pamaso pao; kapena adzacizindikira, angakhalendiwo nyumbayopanduka.
4 Uziturutsa akatundu ako usana pamaso pao, ngati a pa ulendo wa kundende; ndipo madzulo uzituruka wekha pamaso pao, monga amaturuka olowa kundende.
5 Udziboolere khoma pamaso pao, nuwaturutsire akatundu pamenepo,