Ezekieli 34 BL92

Aneneratu motsutsa abusa osakhulupirika a anthu a Mulungu

1 Ndipo mau a Yehova anandidzera, akuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, Nenera motsutsa abusa a Israyeli; nenera, nuti nao abusawo, Atero Ambuye Yehova, Tsoka abusa a Israyeli odzidyetsa okha; kodi abusa sayenera kudyetsa nkhosa?

3 Mukudya mafuta, mubvala ubweya, mukupha zonenepa; koma simudyetsa nkhosa.

4 Zofoka simunazilimbitsa; yodwala simunaiciritsa, yotyoka simunailukira chika, yopitikitsidwa simunaibweza, yotayika simunaifuna; koma munazilamulira mwamphamvu ndi moopsa,

5 M'mwemo zinamwazika posowa mbusa, nizinakhala cakudya ca zirombo ziri zonse za kuthengo, popeza zinamwazika.

6 Nkhosa zanga zinasokera ku mapiri ali onse, ndi pa citunda ciri conse cacitali; inde nkhosa zanga zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo panalibe wakuzipwaira kapena kuzifunafuna.

7 Cifukwa cace abusa inu, imvani mau a Yehova:

8 Pali ine, ati Ambuye Yehova, zedi, popeza nkhosa zanga zinakhala nyama, ndi nkhosa zanga zinakhala cakudya ca zirombo zonse za kuthengo, cifukwa kunalibe mbusa, ndi abusa anga sanafunafuna nkhosa zanga, koma abusawo anadzidyetsa okha, osadyetsa nkhosa zanga;

9 cifukwa cace, abusa inu, imvani mau a Yehova:

10 Atero Ambuye Yehova, Taonani, Ine ndiipidwa nao abusa, ndidzafunsa nkhosa zanga pa dzanja lao, ndi kuwaletsa asadyetsenso nkhosazo, ngakhale kudzidyetsa okha sadzacitanso; ndipo ndidzalanditsa nkhosa zanga pakamwa pao, zisakhale cakudya cao.

11 Pakuti atero Ambuye Yehova, Taonani, Ine, Inedi ndidzapwaira nkhosa zanga ndi kuzifunafuna.

12 Monga mbusa afunafuna nkhosa zace tsiku lokhala iye pakati pa nkhosa zace zobalalika, mamwemo ndidzafunafuna nkhosa zanga; ndipo ndidzawalanditsa m'malo monse anabalalikamo tsiku la mitambo ndi la mdima.

13 Ndipo ndidzaziturutsa mwa mitundu ya anthu, ndi kuzisonkhanitsa m'maiko, ndi kulowa nazo m'dziko lao; ndipo ndidzazidyetsa pa mapiri a Israyeli, patimitsinje, ndi ponse pokhala anthu m'dziko.

14 Ndidzazidyetsa podyetsa pabwino; ndi pa mapiri atali a Israyeli padzakhala kholo lao, apo adzagona m'khola mwabwino, nadzadya podyetsa pokometsetsa pa mapiri a Israyeli.

15 Ine ndekha ndidzadyetsa nkhosa zanga, ndi kuzigonetsa, ati Ambuye Yehova.

16 Ndidzafuna yotayika, ndi kubweza yopitikitsidwa, ndi kulukira chika yotyoka mwendo, ndi kulimbitsa yodwalayo; koma yanenepa ndi yolimba ndidzaziononga, ndidzazidyetsa ndi ciweruzo.

17 Ndipo inu, gulu langa, atero Ambuye Yehova, ndiweruza pakati pa zoweta ndi zoweta, nkhosa zamphongo ndi atonde.

18 Kodi cikuceperani, kuti mwadya podyetsa pabwino? muyenera kodi kupondereza ndi mapazi anu podyera panu potsala? muyenera kumwa madzi ndikha, ndi kubvundulira otsalawo ndi mapazi anu?

19 Ndi nkhosa zanga zidye kodi zoponderezeka ndi mapazi anu, ndi kumwa zobvunduliridwa ndi mapazi anu?

20 Cifukwa cace atero nao Ambuye Yehova, Taonani, Ine, Inedi ndidzaweruza pakati pa zoweta zonenepa, ndi zoweta zoonda.

21 Popeza mukankha ndi nthiti ndi phewa, nimugunda zodwala zonse ndi nyanga zanu, mpaka mwazibalalitsa kubwalo,

22 cifukwa cace ndidzapulumutsa gulu langa lisakhalenso cakudya; ndipo ndidzaweruza pakati pa zoweta ndi zoweta.

23 Ndipo ndidzaziutsira mbusa mmodzi; iye adzazidyetsa, ndiye mtumiki wanga Davide, iye adzazidyetsa, nadzakhala mbusa wao.

24 Ndipo Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wao, ndi mtumiki wanga Davide kalonga pakati pao; Ine Yehova ndanena.

25 Ndipo ndidzapangana nazo pangano la mtendere, ndi kuleketsa zirombo zoipa m'dzikomo; ndipo zidzakhala mosatekeseka m'cipululu, ndi kugona kunkhalango.

26 Pakuti ndidzaika izi ndi miraga yozungulira citunda canga; zikhale mdalitso; ndipo ndidzabvumbitsa mibvumbi m'nyengo yace, padzakhala mibvumbi ya madalitso.

27 Ndi mitengo ya kuthengo idzapereka zobala zao, ndi nthaka idzapereka zipatso zace, ndipo adzakhazikika m'dziko mwao; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, nditadula zomangira goli lao, ndi kuwalanditsa m'manja mwa iwo akuwatumikiritsa.

28 Ndipo sadzakhalanso cakudya ca amitundu, ndi cirombo ca kuthengo sicidzawadyanso; koma adzakhala osatekeseka, opanda wina wakuwaopsa.

29 Ndipo ndidzawautsira mbeu yomveka, ndipo sadzacotsedwanso ndi njala m'dzikomo, kapena kusenzanso manyazi a amitundu.

30 Ndipo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wao ndiri nao, ndi kuti iwo, nyumba ya Israyeli, ndiwo anthu anga, ati Ambuye Yehova.

31 Ndipo inu nkhosa zanga, nkhosa za pabusa panga, ndinu anthu, ndi Ine ndine Mulungu wanu, ati Ambuye Yehova.