56 Ndipo sunakamba za mbale wako Sodomu pakamwa pako tsiku la kudzikuza kwako;
57 cisanabvundukuke coipa cako monga nthawi ya citonzo ca ana akazi a Aramu, ndi onse akumzungulira iye, ana akazi a Afilisti akupeputsa pozungulira ponse.
58 Wasenza coipa cako ndi zonyansa zako, ati Yehova.
59 Pakuti atero Ambuye Yehova, Ndidzacita ndi iwe monga umo unacitira; popeza wapepula lumbiro ndi kutyola pangano.
60 Koma ndidzakumbukila Ine pangano langa ndi iwe m'masiku a ubwana wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha nawe.
61 Pamenepo udzakumbukila njira zako ndi kucita manyazi, pakulandira abale ako akuru ndi ang'ono; ndipo ndidzakupatsa awa akhale ana ako akazi, angakhale sali a pangano lako.
62 Pakuti ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova;