Ezekieli 45:1-7 BL92

1 Ndipo pogawa dziko likhale calowa cao, mupereke copereka kwa Yehova, ndico gawo lopatulika la dziko; m'litali mwace likhale la mabango zikwi makumi awiri mphambu zisanu, ndi kupingasa kwace zikwi makumi awiri; likhale lopatulika m'malire ace onse pozungulira pace.

2 Kutengako malo opatulika akhale nayo mikono mazana asanu m'litali mwace, ndi mazana asanu kupingasa kwace, lamphwamphwa pozungulira pace; ndi pabwalo pace poyera pozungulira pace mikono makumi asanu.

3 Ndipo kuyambira poyesedwapo uyese zikwi makumi awiri mphambu zili sanu m'litali mwace, ndi zikwi khumi kupingasa kwace; m'menemo ndimo mukhale malo opatulika, ndiwo opatulika, ndiwo opatulikitsa.

4 Ndilo gawo lopatulika la dziko, ndilo la ansembe atumiki a malo opatulika, amene ayandikira kutumikira Yehova; apo ndipo amange nyumba zao, likhale malo a pa okha a: kwa malo opatulika.

5 Ndipo zikwi makumi awiri mphambu zisanu m'litali mwace, ndi zikwi khumi kupingasa kwace, ndilo gawo la Alevi, atumiki a kacisi; likhale lao lao la midzi yokhalamo.

6 Ndipo dziko lace la mudziwo mulipereke la zikwi zisanu kupingasa kwace, ndi zikwi makumi awiri mphambu zisanu m'litali mwace, pa mbali ya cipereko copatulika, ndilo la nyumba yonse ya Israyeli.

7 Ndipo kalonga adzakhala nalo gawo lace mbali yina ndi mbali inzace ya cipereko copatulika, ndi ya dziko la mudzi, kutsogolo kwa cipereko copatulika, ndi kutsogolo kwa dziko la mudzi, mbali ya kumadzulo kumadzulo, ndi mbali ya kum'mawa kum'mawa; ndi m'litali mwace mudzalingana ndi limodzi la magawo, kuyambira ku malire a kumadzulo kufikira malire a kum'mawa.