4 Ndi ana amuna a Yavani: Elisa, ndi Tarisisi, ndi Kitimu, ndi Dodanimu.
5 Amenewo ndipo anagawa zisi za amitundu m'maiko mwao, onse amene monga mwa cinenedwe cao; ndi mwa mabanja ao, ndi m'mitundu yao.
6 Ndi ana amuna a Hamu: Kusi, ndi Mizraimu, ndi Puti, ndi Kanani.
7 Ndi ana amuna a Kusi: Seba, ndi Havila, ndi Sabita, ndi Raama, ndi Sabiteka; ndi ana a Raama: Sheba ndi Dedane.
8 Ndipo Kusi anabala Nimrode; ndipo iye anayamba kukhala wamphamvu pa dziko lapansi.
9 Iye ndiye mpalu wamphamvu pamaso pa Yehova: cifukwa cace kunanenedwa, Monga Nimrode mpalu wamphamvu pamaso pa Yehova.
10 Ndipo kuyamba kwace kwa ufumu wace kunali Babele, ndi Ereke, ndi Akadi, ndi Kaline, m'dziko la Sinara.