15 cifukwa kuti dziko lonse limene ulinkuona, ndidzakupatsa iwe ndi mbeu yako nthawi yonse.
16 Ndipo ndidzayesa mbeu yako monga pfumbi lapansi: cotere kuti ngati munthu angathe kuwerenga pfumbi lapansi, comweconso mbeu yako idzawerengedwa.
17 Tauka, nuyendeyendc m'dzikoli m'litari mwace ndi m'mimba mwace; cifukwa kuti ndidzakupatsa iwe limenelo.
18 Ndipo Abramu anasuntha hema wace nafika nakhala pa mitengo yathundu ya pa Mamre, imene iri m'Hebroni, nammangira Yehova kumeneko guwa la nsembe.