1 Ndipo Yehova anamuonekera iye pa mtengo yathundu ya ku Mamre, pamene anakhala pa khomo la hema wace pakutentha dzuwa.
2 Ndipo anatukula maso ace, nayang'ana, taonani, anthu atatu anaima pandunji pace; pamene anaona iwo, anawathamangira kucoka ku khomo la hema kukakomana nao, nawerama pansi, nati,
3 Mbuyanga, ngatitu ndikapeza ufulu pamaso panu, musapitiriretu pa kapolo wanu;
4 nditengetu madzi pang'ono, ndikusambitseni mapazi anu, mupumule pansi pa mtengo;