10 Ndipo Yakobo anacoka m'Beereseba, nanka ku Harana.
11 Ndipo anafika kumalo, nagona kumeneko usiku, cifukwa lidalowa dzuwa: ndipo anatenga mwala wa kumeneko, nauika pansi pa mutu wace, nagona tulo kumeneko.
12 Ndipo analota, taonani, makwerero anaima pansi, pamwamba pace ndipo padafikira kumwamba: ndipo, taonani, amithenga a Mulungu analinkukwera, analinkutsika pamenepo.
13 Taonani, Yehova anaima pamwamba pace, nati, Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu atate wako, ndi Mulungu wa Isake; dziko limene ulinkugonamo ndidzakupatsa Iwe ndi mbeu zako;
14 mbeu zako zidzakhala monga pfumbi lapansi, ndipo udzabalalikira kumadzulo ndi kum'mawa ndi kumpoto ndi kumwera: mwa iwe ndi mu mbeu zako mabanja onse a dziko lapansi adzadalitsidwa.
15 Taonani, Ine ndiri pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakusunga iwe konse kumene upitako, ndipo ndidzakubwezanso iwe ku dziko lino; cifukwa kuti sindidzakusiya iwe, kufikira kuti nditacita cimene ndanena nawe.
16 Ndipo Yakobo anauka m'tulo tace, nati, Ndithu, Yehova ali mommuno; ndipo sindinadziwe.