38 Ndipo Sauli anamwalira, ndipo Baal-hanani mwana wamwamuna wa Akibori analamulira m'malo mwace.
39 Ndipo Baal-hanani mwana wamwamuna wa Akibori anamwalira, ndipo Hadari analamulira m'malo mwace; dzina la mudzi wace ndi Pau; ndipo dzina la mkazi wace ndi Mehetabeli, mwana wamkazi wa Matiredi, mwana wamkazi wa Me-zahabi.
40 Maina a mafumu obadwa kwa Esau, monga mabanja ao, monga malo ao, monga maina ao ndi awa: mfumu Timna, mfumu Aliva, mfumu Jeteti:
41 mfumu Oholibama, mfumu Ela, mfumu Pinoni;
42 mfumu Kenazi, mfumu Temani, mfumu Mibezari;
43 mfumu Magidieli, mfumu Iramu; amenewa ndi mafumu a Edomu, monga mwa kukhala kwao m'dziko lokhala laolao. Uyo ndiye Esau atate wao wa Aedomu.