5 Masiku onse a cowinda cace cakusala, lumo lisapite pamutu pace; kufikira adatha masikuwo adadzipatulira kwa Yehova, azikhala wopatulika; aleke nzera za tsitsi lace zimeretu.
6 Masiku onse akudzipatulira kwa Yehova asayandikize mtembo.
7 Asadzidetse ndi atate wace, kapena mai wace, mbale wace, kapena mlongo wace, akafa iwowa; popeza cowindira Mulungu wace ciri pamutu pace.
8 Masiku onse a kusala kwace akhala wopatulikira kwa Yehova.
9 Munthu akafa cikomo pali iye, ndipo akadetsa mutu wace wowinda; pamenepo azimeta mutu wace tsiku la kumyeretsa kwace, tsiku lacisanu ndi ciwiri aumete.
10 Ndipo tsiku lacisanu ndi citato adze nazo njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, kwa wansembe, ku khomo la cihema cokomanako;
11 ndipo wansembe akonze imodzi nsembe yaucimo, ndi yina nsembe yopsereza, namtetezere popeza anacimwa nao mtembowo; ndipo apatulire mutu wace tsiku lomwelo.