25 Pakuti Ine ndine Yehova, ndidzanena, ndi mau ndidzanenawo adzacitika, osazengerezekanso; pakuti m'masiku anu, nyumba yopanduka inu, ndidzanena mau ndi kuwacita, ati Yehova Mulungu.
26 Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,
27 Wobadwa ndi munthu iwe, taona, iwo a nyumba ya Israyeli akuti, masomphenya awaona ndiwo a masiku ambiri: ndipo anenera za nthawi ziri kutali,
28 Cifukwa cace uziti nao, Atero Ambuye Yehova, Palibe amodzi a mau anga adzazengerezekanso; koma mau ndidzanenawo adzacitika, ati Ambuye Yehova.