1 Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,
2 Wobadwa ndi munthu iwe, Dziwitsa Yerusalemu zonyansa zace, nuziti,
3 Atero Ambuye Yehova kwa Yerusalemu, Ciyambi cako ndi kubadwa kwako ndiko ku dziko la Akanani; atate wako anali M-amori, ndi mai wako Mhiti.
4 Ndipo za kubadwa kwako, tsiku lobadwa iwe sanadula ncofu yako, sanakuyeretsa ndi kukusambitsa ndi madzi, sanakuthira mcere konse, kapena kukukulunga m'nsaru ai.