7 Ndinakucurukitsa ngati mphundu za kumunda; ndipo unathululuka ndi kukula kufikira wakongola nkhope, maere ako anamera, ndi tsitsi lako linamera; koma unali wamarisece ndi wausiwa.
8 Ndipo popita Ine panali iwepo ndi kukupenya, taona nyengo yako ndiyo nyengo yakukondana; pamenepo ndinakupfunda copfunda canga, ndi kuphimba umarisece wako; inde ndinakulumbirira ndi kupangana nawe, ati Ambuye Yehova, ndipo unakhala wanga.
9 Ndipo ndinakusambitsa ndi madzi, inde ndinakutsuka kukucotsera mwazi wako, ndi kukudzoza mafuta.
10 Ndinakubvekanso ndi nsaru zopikapika, ndi kukubveka nsapato za cikopa ca katumbu; ndinakuzenenga nsaru yabafuta, ndi kukuphimba ndi nsaru yasilika.
11 Ndinakukometseranso ndi zokometsera, ndi kuika zigwinjiri m'manja mwako, ndi unyolo m'khosi mwako.
12 Momwemo ndinaika cipini m'mphuno mwako, ndi maperere m'makutu mwako, ndi korona wokongola pamutu pako.
13 Ndipo unadzikometsera ndi golidi, ndi siliva, ndi cobvala cako ndi bafuta ndi silika ndi yopikapika; unadya ufa wosalala, ndi uci, ndi mafuta; ndipo unali wokongola woposa ndithu, ndipo unapindula-pindula kufikira unasanduka ufumu.