4 Taonani, miyoyo yonse ndi yanga, monga moyo wa atate momwemonso moyo wa mwana, ndiyo yanga; moyo wocimwawo ndiwo udzafa.
5 Koma munthu akakhala wolungama, nakacita ciweruzo ndi cilungamo,
6 wosadya pamapiripo, wosakweza maso ace ku mafano a nyumba ya Israyeli, wosaipsa mkazi wa mnansi wace, kapena kuyandikira mkazi ataoloka,
7 wosasautsa munthu ali yense, koma wambwezera wangongole cigwiriro cace, wosatenga zofunkha, anampatsa wanjala cakudya cace, nabveka wamarisece ndi cobvala,
8 wosapereka molira phindu, wosatenga coonjezerapo wobweza dzanja lace lisacite cosalungama, woweruza zoona pakati pa munthu ndi mnzace,
9 amayenda m'malemba anga, nasunga maweruzo anga kucita cokhulupirika; iye ndiye wolungama, adzakhala ndi moyo ndithu, anena Ambuye Yehova.
10 Akabala mwana ndiye mkhungu, wokhetsa mwazi, wocita cimodzi ca izi,