1 Ndipo iwe, takwezera akalonga a Israyeli nyimbo ya maliro,
2 uziti, Mai wako ndi ciani? Mkango waukazi unabwanthama mwa mikango, unalera ana ace pakati pa misona.
3 Ndipo unalera mmodzi wa ana ace, iye nasanduka msona, unaphunzira kugwira nyama, unalusira anthu.
4 Mitundu ya anthu idamva mbiri yace, unagwidwa m'mbuna mwao; ndipo anadza nao ndi zokowera ku dziko la Aigupto.
5 Pakuona tsono waukaziwo, kuti unalindirira, ndi kuti ciyembekezo cace cidatha, unatenga wina wa ana ace, numsandutsa msona.