2 Ndipo kalonga azilowera njira ya ku khonde la cipataco, kunja kwace, naime ku nsanamira ya cipata; ndipo ansembe akonze nsembe yace yopsereza, ndi nsembe zace zoyamika, nalambire iye ku ciundo ca cipata; atatero aturuke; koma pacipata pasatsekedwe mpaka madzulo.
3 Ndipo anthu a m'dziko alambire pa citseko ca cipata ici pamaso pa Yehova pamasabata, ndi pokhala mwezi.
4 Ndipo nsembe yopsereza imene kalonga azipereka kwa Yehova pa Sabata ndiyo ana a nkhosa asanu ndi mmodzi opanda cirema, ndi nkhosa yamphongo yopanda cirema,
5 ndi nsembe yaufa ikhale efa wa pa nkhosa yamphongo, ndi nsembe ya ufa wa pa ana a nkhosa, monga akhoza kupatsa; ndi hini a wa mafuta wa paefa.
6 Ndipo nsembe ya tsiku lokhala mwezi ikhale mwana wa ng'ombe wopanda cirema, ndi ana a nkhosa asanu ndi mmodzi, ndi nkhosa yamphongo, zikhale zopanda cirema;
7 ndipo akonze nsembe yaufa, efa wa pa ng'ombe, ndi efa wa pa nkhosa yamphongo, ndi pa ana a nkhosa, monga akhoza; ndi hini wa mafuta wa paefa.
8 Ndipo polowa kalonga azilowera njira ya ku khonde la cipata, naturuke njira yomweyo.