2 Pamenepo anaturuka nane njira ya ku cipata ca kumpoto, nazungulira nane njira yakunja kumka ku cipata cakunja, njira ya ku cipata coloza kum'mawa; ndipo taonani, panaturuka madzi pa mbali ya kulamanja.
3 Poturuka munthuyu kumka kum'mawa ndi cingwe coyesera m'dzanja lace, anayesa mikono cikwi cimodzi, nandipititsa pamadzi, madzi oyesa m'kakolo.
4 Nayesanso cikwi cimodzi, nandipititsa pamadzi, madzi oyesa m'maondo. Nayesanso cikwi cimodzi, nandipititsa pamadzi, madzi oyesa m'cuuno.
5 Atatero anayesanso cikwi cimodzi, ndipo mtsinje wosakhoza kuoloka ine, popeza madzi adakula, madzi osambira, mtsinje wosaoloka munthu.
6 Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, waona ici? Nanditenga kundikwezetsa ndi mtsinje.
7 Nditabwera tsono, taonani, pa gombe la mtsinjewo mitengo yambirimbiri tsidya lino ndi lija.
8 Pamenepo anati kwa ine, Madzi awa aturukira ku dera la kum'mawa, natsikira kucidikha, nayenda kunyanja; atathira kunyanja akonzeka madzi ace.