10 Ndipo Efroni anakhala pakati pa ana a Heti: ndipo Efroni Mhiti anayankha Abrahamu alinkumva ana a Heti, onse amene analowa pa cipata ca mudzi wace, kuti,
11 Iai, mfumu, mundimvere ine; munda ndikupatsani inu, ndi phanga liri m'menemo ndikupatsani inu, pamaso pa ana a anthu anga ndikupatsani inu; ikani wakufa wanu.
12 Ndipo Abrahamu anawerama pamaso pa anthu a m'dzikomo.
13 Ndipo ananena kwa Efroni alinkumva anthu a m'dzikomo, kuti, Koma ngati ufuna, undimveretu ine: ndidzakupatsa iwe mtengo wace wa munda; uulandire kwa ine, ndipo ndidzaika wakufa wanga m'menemo.
14 Ndipo Efroni anamyankha Abrahamu, nati kwa iye,
15 Mfumu, mundimvere ine; kadziko ka mtengo wace wa masekele a siliva mazana anai, ndiko ciani pakati pa ine ndi inu? ikani wakufa wanu.
16 Ndipo Abrahamu anamvera Effoni, ndipo Abrahamu anamuyesera Efroni ndalama zimene ananena alinkumva ana a Heti, masekele a siliva mazana anai, ndalama zomwezo agulana nazo malonda.