14 Ndipo Rubeni ananka masiku akudula tirigu, napeza zipatso za mankhwala a cikondi m'thengo, nazitengera kwa amace Leva, Ndipo Rakele anati kwa Leya, Undipatseko mankhwala a mwana wako.
15 Ndipo iye anati kwa Rakele, Kodi mpacabe kuti iwe wacotsa mwamuna wanga? Kodi ufuna kucotsanso mankhwala a mwana wanga? Rakele ndipo anati, Cifukwa cace iye adaagona nawe usiku uno cifukwa ca mankhwala a mwana wako.
16 Ndipo Yakobo anadza madzulo kucokera kumunda, ndipo Leya ananka kukomana naye, nati, Ulowe kwa ine cifukwa ndakulipilira iwe ndi mankhwala a mwana wanga. Ndipo anagona naye usiku womwewo.
17 Ndipo Mulungu anamvera Leya, ndipo anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna wacisanu.
18 Ndipo Leya anati, Mulungu wandipatsa ine mphotho yanga, cifukwa ndapatsa mdzakazi wanga kwa mwamuna wanga: namucha dzina lace lsakara.
19 Ndipo Leya anatenganso pakati nambalira Yakobo mwana wamwamuna wacisanu ndi cimodzi.
20 Ndipo Leya anati, Mulungu anandipatsa ine mphatso yabwino; tsopane mwamuna wanga adzakhala ndi ine, cifukwa ndambalira iye ana amuna asanu ndi mmodzi; ndipo anamucha dzina lace Zebuloni.