4 Ndipo Esau anathamangira kukomana naye namfungatira, nagwa pankhope pace, nampsompsona; ndipo analira iwo.
5 Ndipo anatukula maso ace nawaona akazi ndi ana; nati, Ndani awa ali ndi iwe? Ndipo iye anati, Ndiwo ana amene Mulungu anakomera mtima kumpatsa kapolo wanu.
6 Ndipo adzakazi anayandikira ndi ana ao, nawerama pansi.
7 Ndiponso Leya ndi ana ace anayandikira nawerama pansi: pambuyo pace anayandikira Yosefe ndi Rakele, nawerama pansi,
8 Ndipo anati, Nanga khamu lonse limene ndinakomana nalo nlotani? Ndipo anati, Kuti ndipeze ufulu pamaso pa mbuyanga.
9 Ndipo Esau anati, Zanga zindifikira; mbale wanga, khala nazo zako iwe wekha.
10 Ndipo! Yakobo anati, Iaitu, ngatitu ndapeza ufulu pamaso panu, mulandire mphatso yanga pa dzanja langa; pakuti popeza ndinaona nkhope yanu, monga anthu aona nkhope ya Mulungu, ndipo inu mwanelibvomereza ine.