3 Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.
4 Koma nyama, m'mene muli moyo wace, ndiwo mwazi wace, musadye.
5 Zoonatu mwazi wanu wa miyoyo yanu ndidzafuna; pa dzanja la zinyama zonse ndidzaufuna: ndi pa dzanja la munthu, pa dzanja la mbale wace wa munthu ndidzaufuna moyo wa munthu.
6 Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wace udzakhetsedwa: cifukwa m'cifanizo ca Mulungu Iye anampanga munthu.
7 Ndi inu, mubalane, mucuruke; muswane pa dziko lapansi, nimucuruke m'menemo.
8 Ndipo Mulungu ananena kwa Nowa ndi kwa ana ace pamodzi naye, kuti,
9 Ndipo Ine, taonani, Ine ndikhazikitsa pangano langa pamodzi ndi inu, ndi mbeu zanu pambuyo panu;