43 Ndi pomwepo mudzakumbukila njira zanu, ndi zonse mudazicita ndi kudzidetsa nazo, ndipo mudzakhala onyansa pamaso pa inu nokha, cifukwa ca zoipa zanu zonse mudazicita.
44 M'mwemo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova nditacita nanu cifukwa ca dzina langa, si monga mwa njira zanu zoipa, kapena monga mwa macitidwe anu obvunda, nyumba ya Israyeli inu, ati Ambuye Yehova.
45 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
46 Wobadwa ndi munthu iwe, lozetsa nkhope yako njira ya kumwera, nubenthulire mau kumwera, nunenere nkhalango ya kuthengo la kumwera kwa Yuda;
47 nuziti kwa nkhalango ya kumwera kwa Yuda, Tamvera mau a Yehova, Atero Ambuye Yehova, Taona ndidzayatsa moto mwa iwe, udzanyeketsa mtengo uli wonse wauwisi mwa iwe, ndi mtengo uli wonse wouma; malawi amoto sadzazimika, ndi nkhope zonse kuyambira kumwera kufikira kumpoto zidzapsa nao.
48 Ndi anthu onse adzaona kuti Ine Yehova ndinauyatsa, sudzazimika.
49 Pamenepo ndinati, Ha, Ambuye Yehova! anandinena, Wonena mafanizo uyu.