1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
2 Wobadwa ndi munthu iwe, panali akazi awiri, mai wao ndi mmodzi;
3 ndipo anacita cigololo iwo m'Aigupto, anacita cigololo m'ubwana wao; pomwepo anthu anasindikiza maere ao, pomweponso anakhudza nsonga za maere za unamwali wao.
4 Ndipo maina ao ndiwo Ohola wamkuru, ndi Oholiba mng'ono wace; nakhala anga, nabala ana amuna ndi akazi. Ndipo maina ao, Samariya ndiye Ohola, ndi Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Koma Ohola anacita cigololo pamene anali wanga, anaumirira mabwenzi ace Aasuri oyandikizana naye;