4 Ndipo maina ao ndiwo Ohola wamkuru, ndi Oholiba mng'ono wace; nakhala anga, nabala ana amuna ndi akazi. Ndipo maina ao, Samariya ndiye Ohola, ndi Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Koma Ohola anacita cigololo pamene anali wanga, anaumirira mabwenzi ace Aasuri oyandikizana naye;
6 obvala cibakuwa, ziwanga, ndi akazembe, onsewo anyamata ofunika, anthu oyenda pa akavalo.
7 Ndipo anacita nao zigololo zace, ndiwo anthu osankhika a ku Asuri onsewo, ndipo ali onse anawaumirira anadziipsa nao mafano ao.
8 Sanalekanso zigololo zace zocokera ku Aigupto, pakuti anagona naye m'unamwali wace, nakhudza maere a unamwali wace, namtsanulira cigololo cao.
9 Cifukwa cace ndampereka m'dzanja la mabwenzi ace, m'dzanja la Aasuri amene anawaumirira.
10 Iwowa anabvula umarisece wace, anatenga ana ace amuna ndi akazi, namupha iyeyu ndi lupanga; ndi dzina lace linamveka mwa akazi atamcitira maweruzo.