1 Dzanja la Yehova linandikhalira, ndipo anaturuka nane mu mzimu wa Yehova, nandiika m'kati mwa cigwa, ndico codzala ndi mafupa;
2 ndipo anandipititsa pamenepo pozungulira ponse, ndipo taonani, anali aunyinji pacigwa pansi, ndipo anaumitsitsa.
3 Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, mafupa awa nkukhala ndi moyo kodi? Ndipo ndinati, Ambuye Yehova, mudziwa ndinu.
4 Pamenepo anati kwa ine, Nenera kwa mafupa awa, nuti nao, Mafupa ouma inu, imvani mau a Yehova.