17 Anayesa mbali ya kumpoto mabango mazana asanu, kuyesa ndi bango loyesera, pozungulira pace.
18 Anayesa mbali ya kumwela mabango mazana asanu, kuyesa ndi bango loyesera,
19 Anatembenukira ku mbali ya kumadzulo, nayesa mabango mazana asanu ndi bango loyesera.
20 Analiyesa mbali zace zinai, linali nalo linga pozungulira pace, utali wace mazana asanu, citando cace mazana asanu, kusiyanitsa pakati pa zopatulika ndi zawamba.