Ezekieli 48:16-22 BL92

16 Ndi miyeso yace ndi iyi: mbali ya kumpoto, mabango zikwi zinai mphambu mazana asanu; ndi mbali ya kumwela, zikwi zinai mphambu mazana asanu; ndi mbali ya kummawa, zikwi zinai mphambu mazana asanu; ndi mbali ya kumadzulo, zikwi zinai mphambu mazana asanu.

17 Ndipo mudziwo ukhale ndi busa lace; kumpoto mabango mazana awiri mphambu makumi asanu, kumwela mazana awiri mphambu makumi asanu, ndi kum'mawa mazana awiri mphambu makumi asanu, ndi kumadzulo mazana awiri mphambu makumi asanu.

18 Ndipo madera otsalawo m'litali mwace alingane ndi copereka copatulika, ndico zikwi khumi kum'mawa, ndi zikwi khumi kumadzulo, alingane ndi copereka copatulika; ndi zipatso zace zikhale za cakudya ca iwo ogwira nchito m'mudzi.

19 Iwo ogwira nchito m'mudzi mwa mafuko onse a Israyeli alimeko.

20 Copereka conse ndico mabango zikwi makumi awiri mphambu zisanu m'litali mwace, zikwi makumi awiri mphambu zisanu kupingasa kwace; mucipereke copereka copatulika camphwamphwa, pamodzi ndi dziko la mudziwo.

21 Ndipo madera ena otsalawo ndiwo a kalonga, mbali yina ndi yina ya copereka copatulika ndi ya dziko la mudzi, kutsogolo kwa zikwi makumi awiri mphambu zisanu za copereka ku malire a kum'mawa, ndi kumadzulo kutsogolo kwa zikwi makumi awiri mphambu zisanu ku malire a kumadzulo, pandunji pa magawo enawo ndiwo ca kalonga; ndipo copereka copatulika ndi malo opatulika a kacisi zidzakhala pakati pace.

22 Kuyambira tsono dziko la Alevi kufikira dziko la mudzi, ndiwo a pakati pa magawo ace a kalonga, pakati pa malire a Yuda ndi malire a Benjamini, kukhale kwa kalonga.